Masalimo 105:1-45 OCCL
[1] Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita. [2] Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa. [3] Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere. [4] Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse. [5] Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka, [6] inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake. [7] Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi. [8] Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse, [9] pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake. [10] Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya: [11] “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.” [12] Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo, [13] ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina. [14] Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo: [15] “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.” [16] Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse; [17] Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo. [18] Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo, [19] mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona. [20] Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo. [21] Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo, [22] kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu. [23] Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu. [24] Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo; [25] amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake. [26] Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha. [27] Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu. [28] Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova. [29] Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife. [30] Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo. [31] Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse. [32] Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse; [33] Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo. [34] Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka; [35] zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo. [36] Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse. [37] Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka. [38] Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo. [39] Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku. [40] Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba. [41] Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu. [42] Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake. [43] Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe; [44] Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira, [45] kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
