Masalimo 107:1-43 OCCL
[1] Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha. [2] Owomboledwa a Yehova anene zimenezi amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani, [3] iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko, kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera. [4] Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu, osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako. [5] Iwo anamva njala ndi ludzu, ndipo miyoyo yawo inafowokeratu. [6] Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo. [7] Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka kupita ku mzinda umene anakakhazikikako. [8] Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse, [9] pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino. [10] Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu, amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo, [11] pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba. [12] Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga; anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize. [13] Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo. [14] Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu ndipo anadula maunyolo awo. [15] Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse, [16] pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo. [17] Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira, ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo. [18] Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa. [19] Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo. [20] Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa; anawalanditsa ku manda. [21] Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu. [22] Apereke nsembe yachiyamiko ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe. [23] Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi; Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu. [24] Anaona ntchito za Yehova, machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya. [25] Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho imene inabweretsa mafunde ataliatali. [26] Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya; pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka. [27] Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera; anali pa mapeto a moyo wawo. [28] Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo. [29] Yehova analetsa namondwe, mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa. [30] Anali osangalala pamene kunakhala bata, ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna. [31] Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu. [32] Akuze Iye mu msonkhano wa anthu ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu. [33] Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu, akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma, [34] ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere, chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko. [35] Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda; [36] kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako, ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko. [37] Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa ndipo anakolola zipatso zochuluka; [38] Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri, ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe. [39] Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni; [40] Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira. [41] Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo ngati magulu a nkhosa. [42] Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala, koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo. [43] Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.
