1 Mbiri 2:1-55 OCCL
[1] Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni, [2] Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri. [3] Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha. [4] Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu. [5] Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli. [6] Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu. [7] Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa. [8] Mwana wa Etani anali Azariya. [9] Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai. [10] Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda. [11] Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi, [12] Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese. [13] Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea, [14] wachinayi Netaneli, wachisanu Radai, [15] wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide. [16] Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli. [17] Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli. [18] Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni. [19] Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri. [20] Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli. [21] Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu. [22] Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi. [23] (Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi. [24] Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa. [25] Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya. [26] Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu. [27] Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri. [28] Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri. [29] Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi. [30] Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana. [31] Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai. [32] Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana. [33] Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli. [34] Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha. [35] Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi. [36] Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi, [37] Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi, [38] Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya, [39] Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa, [40] Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu, [41] Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama. [42] Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni. [43] Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema. [44] Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai. [45] Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri. [46] Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi. [47] Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi. [48] Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana. [49] Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa. [50] Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu, [51] Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera. [52] Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati, [53] ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa. [54] Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori, [55] ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.
