1 Mbiri 1:1-54 OCCL
[1] Adamu, Seti, Enosi [2] Kenani, Mahalaleli, Yaredi, [3] Enoki, Metusela, Lameki, Nowa. [4] Ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. [5] Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi. [6] Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima [7] Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu. [8] Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani [9] Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani. [10] Kusi anali abambo a Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi. [11] Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu, [12] Apaturusi, Akasilu (kumene kunachokera Afilisti) ndi Akafitori. [13] Kanaani anabereka mwana wake wachisamba Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti, [14] Ayebusi, Aamori, Agirigasi [15] Ahivi, Aariki, Asini [16] Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. [17] Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu. Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki. [18] Aripakisadi anabereka Sela ndipo Selayo anabereka Eberi: [19] Eberi anabereka ana aamuna awiri: wina anamutcha Pelegi, chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani. [20] Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera, [21] Hadoramu, Uzali, Dikila [22] Obali, Abimaeli, Seba, [23] Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani. [24] Semu, Aripakisadi, Sela [25] Eberi, Pelegi, Reu [26] Serugi, Nahori, Tera [27] ndi Abramu (amene ndi Abrahamu). [28] Ana a Abrahamu ndi awa: Isake ndi Ismaeli. [29] Zidzukulu zake zinali izi: Nebayoti ndiye anali mwana woyamba wa Ismaeli, kenaka Kedara, Adibeeli, Mibisamu, [30] Misima, Duma, Masa, Hadadi, Tema, [31] Yeturi, Nafisi ndi Kedema. Awa anali ana a Ismaeli. [32] Ana a Ketura mzikazi wa Abrahamu anali awa: Zimurani, Yokisani, Medani, Midiyani, Isibaki ndi Suwa. Ana a Yokisani ndi awa: Seba ndi Dedani [33] Ana aamuna a Midiyani anali, Efai, Eferi, Hanoki, Abida ndi Elida. Onsewa anali zidzukulu za Ketura. [34] Abrahamu anabereka Isake. Ana a Isake anali awa: Esau ndi Israeli. [35] Ana aamuna a Esau anali awa: Elifazi, Reueli, Yeusi, Yolamu ndi Kora. [36] Ana a Elifazi anali awa: Temani, Omari, Zefo, Gatamu ndi Kenazi: Amene anabereka ndi Timna: Amaleki. [37] Ana a Reueli anali awa: Nahati, Zera, Sama ndi Miza. [38] Ana a Seiri anali awa: Lotani, Sobala, Zibeoni, Ana, Disoni, Ezeri ndi Disani. [39] Ana aamuna a Lotani anali awa: Hori ndi Homamu. Timna anali mlongo wake wa Lotani. [40] Ana aamuna a Sobala anali awa: Alivani, Manahati, Ebala, Sefo ndi Onamu. Ana aamuna a Zibeoni anali awa: Ayiwa ndi Ana. [41] Mwana wa Ana anali Disoni. Ana a Disoni anali awa: Hemudani, Esibani, Itirani ndi Kerani [42] Ana aamuna a Ezeri anali awa: Bilihani, Zaavani ndi Yaakani. Ana aamuna a Disani anali awa: Uzi ndi Arani. [43] Awa ndi mafumu amene ankalamulira dziko la Edomu, mfumu iliyonse ya Israeli isanayambe kulamulira kumeneko: Bela mwana wa Beori, mzinda wake ankawutcha Dinihaba. [44] Bela atamwalira, Yobabu mwana wa Zera wochokera ku Bozira analowa ufumu mʼmalo mwake. [45] Yobabu atamwalira, Husamu wochokera ku dziko la Atemani, analowa ufumu mʼmalo mwake. [46] Husamu atamwalira, Hadadi mwana wa Bedadi, amene anagonjetsa Amidiyani mʼdziko la Mowabu, analowa ufumu mʼmalo mwake. Mzinda wake unkatchedwa Aviti. [47] Hadadi atamwalira, Samila wochokera ku Masireka analowa ufumu mʼmalo mwake. [48] Samila atamwalira, Sauli wochokera ku Rehoboti wa ku Mtsinje analowa ufumu mʼmalo mwake. [49] Sauli atamwalira, Baala-Hanani mwana wa Akibori analowa ufumu mʼmalo mwake. [50] Pamene Baala-Hanani anamwalira, Hadadi analowa ufumu mʼmalo mwake. Mzinda wake unkatchedwa Pau, ndipo dzina la mkazi wake linali Mehatabeli mwana wa Matiredi, mwana wamkazi wa Me-Zahabu. [51] Hadadi anamwaliranso. Mafumu a ku Edomu anali: Timna, Aliva, Yeteti, [52] Oholibama, Ela, Pinoni, [53] Kenazi, Temani, Mibezari, [54] Magidieli ndi Iramu. Awa anali mafumu a ku Edomu.
