1 Mbiri 3:1-24 OCCL
[1] Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa: Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli; wachiwiri anali Danieli, amayi ake anali Abigayeli wa ku Karimeli; [2] wachitatu anali Abisalomu, mwana wa Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri; wachinayi anali Adoniya amayi ake anali Hagiti; [3] wachisanu anali Sefatiya, amayi ake anali Abitali; wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila. [4] Ana asanu ndi mmodzi awa a Davide anabadwira ku Hebroni kumene analamulirako zaka zisanu ndi ziwiri ndi miyezi isanu ndi umodzi. Davide analamuliranso mu Yerusalemu kwa zaka 33, [5] ndipo ana amene anabadwira ku Yerusalemuko anali awa: Samua, Sobabu, Natani ndi Solomoni. Ana anayi awa anali a Batisuwa mwana wa Amieli. [6] Anaberekanso Ibihari, Elisua, Elipeleti, [7] Noga, Nefegi, Yafiya, [8] Elisama, Eliada ndi Elifeleti, onse analipo asanu ndi anayi. [9] Onsewa anali ana a Davide, osawerengera ana a azikazi. Ndipo mlongo wawo anali Tamara. [10] Mwana wa Solomoni anali Rehabiamu, Rehabiamu anabereka Abiya, Abiya anabereka Asa, Asa anabereka Yehosafati, [11] Yehosafati anabereka Yehoramu, Yehoramu anabereka Ahaziya, Ahaziya anabereka Yowasi, [12] Yowasi anabereka Amaziya, Amaziya anabereka Azariya, Azariya anabereka Yotamu, [13] Yotamu anabereka Ahazi, Ahazi anabereka Hezekiya, Hezekiya anabereka Manase, [14] Manase anabereka Amoni, Amoni anabereka Yosiya. [15] Ana a Yosiya anali awa: Yohanani mwana wake woyamba, Yehoyakimu mwana wake wachiwiri, Zedekiya mwana wake wachitatu, Salumu mwana wake wachinayi. [16] Ana a Yehoyakimu: Yekoniya ndi Zedekiya mwana wake. [17] Zidzukulu za Yekoniya wa mʼndende zinali izi: mwana wake Silatieli, [18] Malikiramu, Pedaya, Senazara, Yekamiya, Hosama ndi Nedabiya. [19] Ana a Pedaya anali awa: Zerubabeli ndi Simei. Ana a Zerubabeli anali awa: Mesulamu ndi Hananiya. Mlongo wawo anali Selomiti. [20] Panalinso ana ena asanu awa: Hasubu, Oheli, Berekiya, Hasabiya ndi Yusabu-Hesedi. [21] Zidzukulu za Hananiya zinali izi: Pelatiya ndi Yesaiya, ndiponso ana a Refaya, ana a Arinani, ana a Obadiya ndi ana a Sekaniya. [22] Zidzukulu za Sekaniya zinali izi: Semaya ndi ana ake: Hatusi, Igala, Bariya, Neariya ndi Safati. Onse anali asanu ndi mmodzi. [23] Ana a Neariya anali awa: Eliyoenai, Hezekiya ndi Azirikamu. Onse anali atatu. [24] Ana a Eliyoenai: Hodaviya, Eliyasibu, Pelaya, Akubu, Yohanani, Delaya ndi Anani, onse anali asanu ndi awiri.
