Yobu 34:1-37 OCCL
[1] Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti, [2] “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira. [3] Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya. [4] Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino. [5] “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama. [6] Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’ [7] Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi? [8] Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima. [9] Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’ [10] “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa. [11] Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita. [12] Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo. [13] Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse? [14] Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake, [15] zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi. [16] “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena. [17] Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo? [18] Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’ [19] Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake? [20] Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu. [21] “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse. [22] Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko. [23] Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa. [24] Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena. [25] Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika. [26] Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona; [27] Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse. [28] Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo. [29] Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu, [30] kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha. [31] “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso, [32] ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’ [33] Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa. [34] “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti, [35] ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’ [36] Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa! [37] Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
