Yobu 33:1-33 OCCL
[1] “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene. [2] Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa. [3] Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa. [4] Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo. [5] Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse. [6] Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi. [7] Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi. [8] “Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti, [9] ‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa. [10] Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake. [11] Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’ [12] “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu. [13] Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu? [14] Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi. [15] Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi, [16] amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake, [17] kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake, [18] kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga. [19] “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya, [20] kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe. [21] Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera. [22] Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa. [23] “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera, [24] kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’ [25] pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake. [26] Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba. [27] Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga. [28] Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’ [29] “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri, [30] kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo. [31] “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule. [32] Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama. [33] Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”
