Miyambo 19:1-29 OCCL
[1] Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota. [2] Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira. [3] Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova. [4] Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa. [5] Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka. [6] Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense. [7] Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse. [8] Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino. [9] Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka. [10] Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga! [11] Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa. [12] Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu. [13] Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi. [14] Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova. [15] Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala. [16] Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa. [17] Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere. [18] Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake. [19] Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale. [20] Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru. [21] Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike. [22] Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza. [23] Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera. [24] Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake. [25] Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso. [26] Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa. [27] Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru. [28] Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa. [29] Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.
