[1] Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
[2] Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
[3] Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
[4] Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
[5] Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
[6] Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
[7] Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
[8] Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
[9] Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
[10] Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
[11] Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
[12] Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
[13] Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
[14] Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
[15] Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
[16] Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
[17] Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
[18] Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
[19] Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
[20] Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
[21] Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
[22] Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
[23] Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
[24] Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.