[1] Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
[2] Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
[3] Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
[4] Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
[5] Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
[6] Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
[7] Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
[8] Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. Sela
[9] Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
[10] Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
[11] Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
[12] amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
[13] Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
[14] Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
[15] kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
[16] Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
[17] Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
[18] Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.