Masalimo 83:1-18 OCCL

[1] Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu. [2] Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo. [3] Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda. [4] Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.” [5] Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu: [6] Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri, [7] Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo. [8] Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. Sela [9] Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni. [10] Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala. [11] Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna, [12] amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.” [13] Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo. [14] Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri, [15] kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe. [16] Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova. [17] Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi. [18] Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.