Masalimo 82:1-8 OCCL

[1] Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.” [2] “Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa? [3] Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika. [4] Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa. [5] “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka. [6] “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’ [7] Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.” [8] Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.