[1] Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
[2] Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
[3] Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. Sela
[4] Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
[5] Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
[6] Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
[7] Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
[8] Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
[9] pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. Sela
[10] Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
[11] Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
[12] Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.