Masalimo 76:1-12 OCCL

[1] Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli. [2] Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni. [3] Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. Sela [4] Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri. [5] Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake. [6] Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi. [7] Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya? [8] Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete, [9] pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. Sela [10] Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu. [11] Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa. [12] Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.