Masalimo 75:1-10 OCCL

[1] Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa. [2] Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo. [3] Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. Sela [4] Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu. [5] Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’ ” [6] Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu. [7] Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina. [8] Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse. [9] Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo. [10] Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.