Masalimo 7:1-17 OCCL

[1] Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa, [2] mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa. [3] Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa, [4] ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga, [5] pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. Sela [6] Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu. [7] Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako; [8] Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba. [9] Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa. [10] Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima. [11] Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku. [12] Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta. [13] Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto. [14] Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena. [15] Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo. [16] Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe. [17] Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.