Masalimo 6:1-10 OCCL

[1] Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu. [2] Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu. [3] Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti? [4] Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika. [5] Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? [6] Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi. [7] Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga. [8] Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga. [9] Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa. [10] Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.