Masalimo 67:1-7 OCCL

[1] Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire. [2] Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse. [3] Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni. [4] Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi. [5] Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni. [6] Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu. [7] Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.