[1] Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi! [2] Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero. [3] Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu. [4] Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” Sela. [5] Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu. [6] Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye. [7] Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule. [8] Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke; [9] Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke. [10] Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva. [11] Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu. [12] Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka. [13] Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga. [14] Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto. [15] Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. Sela [16] Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira. [17] Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga. [18] Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera; [19] koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga. [20] Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!