[1] Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
[2] Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
[3] Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
[4] Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
[5] Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
[6] Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
[7] Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
[8] Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
[9] Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
[10] Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
[11] Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
[12] Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
[13] Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
[14] Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
[15] Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
[16] Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
[17] Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
[18] Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
[19] Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
[20] Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
[21] Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
[22] Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.