Masalimo 38:1-22 OCCL

[1] Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali. [2] Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira. [3] Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa. [4] Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga. [5] Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo. [6] Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira. [7] Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa. [8] Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima. [9] Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu. [10] Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga. [11] Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane. [12] Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo. [13] Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake; [14] Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha. [15] Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga. [16] Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.” [17] Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse. [18] Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa. [19] Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri. [20] Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino. [21] Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga. [22] Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.