Masalimo 37:1-40 OCCL
[1] Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa; [2] pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga. [3] Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika. [4] Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako. [5] Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi: [6] Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana. [7] Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa. [8] Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa. [9] Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko. [10] Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso. [11] Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu. [12] Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano; [13] koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera. [14] Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama. [15] Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka. [16] Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri; [17] pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama. [18] Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya. [19] Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri. [20] Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi. [21] Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja. [22] Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa. [23] Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake; [24] ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake. [25] Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya. [26] Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika. [27] Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya. [28] Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa; [29] olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya. [30] Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama. [31] Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka. [32] Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo; [33] koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu. [34] Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka. [35] Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake. [36] Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso. [37] Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri. [38] Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe. [39] Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso. [40] Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.
