Masalimo 30:1-12 OCCL

[1] Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine. [2] Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa. [3] Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. [4] Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera. [5] Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa. [6] Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.” [7] Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima. [8] Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo; [9] “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu? [10] Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.” [11] Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe, [12] kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.