[1] Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
[2] Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
[3] Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje.
[4] Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
[5] Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
[6] Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
[7] Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
[8] Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
[9] “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
[10] Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
[11] Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
[12] kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.