Masalimo 29:1-11 OCCL

[1] Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu. [2] Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake. [3] Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu. [4] Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero. [5] Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni. [6] Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati: [7] Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi. [8] Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi. [9] Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!” [10] Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya. [11] Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.