[1] Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
[2] Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” Sela
[3] Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
[4] Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. Sela
[5] Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
[6] Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
[7] Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
[8] Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. Sela