Masalimo 3:1-8 OCCL

[1] Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira! [2] Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” Sela [3] Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula. [4] Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. Sela [5] Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza. [6] Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse. [7] Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa. [8] Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. Sela

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.