Masalimo 3:1-8 OCCL

[1] Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira! [2] Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” Sela [3] Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula. [4] Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. Sela [5] Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza. [6] Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse. [7] Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa. [8] Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. Sela

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.