Masalimo 2:1-12 OCCL

[1] Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu? [2] Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo. [3] Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.” [4] Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo. [5] Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti, [6] “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.” [7] Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako. [8] Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako. [9] Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.” [10] Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi. [11] Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera. [12] Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.