Masalimo 2:1-12 OCCL

[1] Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu? [2] Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo. [3] Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.” [4] Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo. [5] Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti, [6] “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.” [7] Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako. [8] Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako. [9] Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.” [10] Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi. [11] Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera. [12] Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.