[1] Inu Yehova, mfumu ikusangalala mu mphamvu yanu, chimwemwe chake nʼchachikuludi pa kupambana kumene mumapereka! [2] Inu mwayipatsa zokhumba za mtima wake ndipo simunayimane zopempha za pa milomo yake. Sela [3] Inu munayilandira ndi madalitso ochuluka ndipo munayiveka chipewa chaufumu chagolide weniweni pa mutu wake. [4] Iye anakupemphani moyo, ndipo munamupatsa masiku ochuluka kwamuyaya. [5] Kudzera mʼzigonjetso zimene munapereka, ulemerero wake ndi waukulu; Inu mwapereka pa iyo ulemerero ndi ufumu. [6] Zoonadi Inu mwayipatsa madalitso amuyaya, Inu mwayipatsa chisangalalo ndi chimwemwe chimene chili pamaso panu. [7] Pakuti mfumu imadalira Yehova; kudzera mʼchikondi chake chosatha cha Wammwambamwamba, iyo sidzagwedezeka. [8] Dzanja lanu lidzayimitsa adani anu onse; dzanja lanu lamanja lidzagwira adani anu. [9] Pa nthawi ya kuonekera kwanu mudzawasandutsa ngʼanjo yamoto yotentha. Mu ukali wake Yehova adzawameza, ndipo moto wake udzawatha. [10] Inu mudzawononga ana awo pa dziko lapansi, zidzukulu zawo pakati pa anthu. [11] Ngakhale iwo akukonzereni chiwembu mwa kuchenjera kwawo sadzapambana; [12] pakuti mudzawapirikitsa ndipo adzaonetsa misana yawo pamene mudzawaloza ndi mivi yanu. [13] Mukwezeke Inu Yehova mʼmphamvu yanu, ife tidzayimba nyimbo ndi kutamanda mphamvu yanu.