[1] Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze. [2] Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni. [3] Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. Sela [4] Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike. [5] Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse. [6] Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja. [7] Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu. [8] Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili. [9] Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!