[1] Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera. [2] Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse. [3] Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse, [4] amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu, [5] amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu. [6] Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika. [7] Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli. [8] Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka. [9] Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya; [10] satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu. [11] Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa; [12] monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe. [13] Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa; [14] pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi. [15] Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda; [16] koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso. [17] Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo; [18] iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake. [19] Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse. [20] Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake. [21] Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake. [22] Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.