Masalimo 102:1-28 OCCL
[1] Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu. [2] Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga. [3] Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka. [4] Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa. [5] Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha. [6] Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja. [7] Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga. [8] Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero. [9] Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi [10] chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali. [11] Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu. [12] Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse. [13] Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika. [14] Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni. [15] Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu. [16] Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake. [17] Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo. [18] Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova: [19] “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi, [20] kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.” [21] Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu, [22] pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova. [23] Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga. [24] Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse. [25] Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu. [26] Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa. [27] Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha. [28] Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
