Yobu 41:1-34 OCCL
[1] “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe? [2] Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza? [3] Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa? [4] Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya? [5] Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo? [6] Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse? [7] Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba? [8] Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso. [9] Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha. [10] Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine? [11] Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga. [12] “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake. [13] Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho? [14] Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha? [15] Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana; [16] Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake. [17] Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana. [18] Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha. [19] Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto. [20] Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango. [21] Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake. [22] Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha. [23] Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba. [24] Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero. [25] Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa. [26] Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera. [27] Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola. [28] Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya. [29] Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo. [30] Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu. [31] Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta. [32] Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi. [33] Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha. [34] Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
