Yobu 4:1-21 OCCL

[1] Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti, [2] “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula? [3] Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka. [4] Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu. [5] Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha. [6] Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako? [7] “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa? [8] Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo. [9] Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake. [10] Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa. [11] Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana. [12] “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake. [13] Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato, [14] ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka. [15] Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo. [16] Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti, [17] ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake? [18] Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa, [19] nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche! [20] Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya. [21] Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.