Yobu 38:1-41 OCCL
[1] Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati: [2] “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru? [3] Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe. [4] “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa. [5] Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli? [6] Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya, [7] pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa? [8] “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko, [9] pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani, [10] pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake. [11] Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’ [12] “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake, [13] kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa? [14] Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala. [15] Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu. [16] “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama? [17] Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani? [18] Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi. [19] “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti? [20] Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko? [21] Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi! [22] “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala, [23] zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo? [24] Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi? [25] Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi, [26] kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu, [27] kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu? [28] Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani? [29] Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba [30] pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa? [31] “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana? [32] Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake? [33] Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi? [34] “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula? [35] Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’ [36] Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu? [37] Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo [38] pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika? [39] “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango [40] pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire? [41] Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
