Yobu 36:1-33 OCCL
[1] Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati: [2] “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu. [3] Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga. [4] Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu. [5] “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake. [6] Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa. [7] Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya. [8] Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso, [9] Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza. [10] Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo. [11] Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala. [12] Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu. [13] “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo. [14] Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo. [15] Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo. [16] “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri. [17] Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani. [18] Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni. [19] Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso? [20] Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka. [21] Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu. [22] “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye? [23] Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’ [24] Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo. [25] Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali. [26] Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika. [27] “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula; [28] mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira. [29] Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake? [30] Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja. [31] Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka. [32] Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna. [33] Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.
