Yobu 13:1-28 OCCL
[1] “Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa. [2] Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. [3] Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu. [4] Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu! [5] Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru. [6] Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga. [7] Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo? [8] Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake? [9] Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu? [10] Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri. [11] Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha? [12] Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi. [13] “Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike. [14] Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu? [15] Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake. [16] Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake! [17] Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena. [18] Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama. [19] Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa. [20] “Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani: [21] Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko. [22] Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe. [23] Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga. [24] Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu? [25] Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma? [26] Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga. [27] Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo. [28] “Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
