[1] Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse. [2] Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo. [3] Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda! [4] Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Amachita bwinotu potamanda iwe! [5] Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni. [6] Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire. [7] Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako? [8] Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa. [9] Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao. [10] Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali. [11] Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva. [12] Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake. [13] Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa. [14] Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi. [15] Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda. [16] Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira. [17] Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.