Numeri 1:1-54 OCCL
[1] Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti, [2] “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi. [3] Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali. [4] Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi. [5] Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni, [6] Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni, [7] Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda, [8] Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara, [9] Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni, [10] Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri; [11] Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini, [12] Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani, [13] Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri, [14] Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi, [15] Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.” [16] Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli. [17] Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa, [18] ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi [19] monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai: [20] Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. [21] Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500. [22] Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. [23] Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300. [24] Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. [25] Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650. [26] Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. [27] Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600. [28] Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. [29] Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400. [30] Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. [31] Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400. [32] Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. [33] Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500. [34] Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. [35] Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200. [36] Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. [37] Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400. [38] Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. [39] Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700. [40] Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. [41] Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500. [42] Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. [43] Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400. [44] Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake. [45] Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo. [46] Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550. [47] Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena. [48] Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, [49] “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli. [50] Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo. [51] Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa. [52] Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake. [53] Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.” [54] Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
