Miyambo 31:1-31 OCCL
[1] Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake: [2] Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro? [3] Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu. [4] Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa [5] kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka. [6] Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa; [7] amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo. [8] Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera. [9] Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka. [10] Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali. [11] Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu. [12] Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa. [13] Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu. [14] Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali. [15] Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito. [16] Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa. [17] Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake. [18] Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse. [19] Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu. [20] Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa. [21] Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda. [22] Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo. [23] Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo. [24] Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda. [25] Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo. [26] Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi. [27] Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe. [28] Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati, [29] “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.” [30] Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa. [31] Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.
