Miyambo 29:1-27 OCCL
[1] Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa. [2] Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula. [3] Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake. [4] Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko. [5] Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake. [6] Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma. [7] Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi. [8] Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali. [9] Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere. [10] Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake. [11] Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira. [12] Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa. [13] Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa. [14] Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse. [15] Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi. [16] Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo. [17] Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako. [18] Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo. [19] Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu. [20] Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula. [21] Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake. [22] Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri. [23] Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu. [24] Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu. [25] Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa. [26] Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi. [27] Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.
