Miyambo 15:1-33 OCCL
[1] Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali. [2] Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru. [3] Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe. [4] Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima. [5] Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo. [6] Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto. [7] Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero. [8] Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima. [9] Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo. [10] Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa. [11] Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! [12] Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru. [13] Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo. [14] Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo. [15] Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse. [16] Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto. [17] Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani. [18] Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu. [19] Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu. [20] Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake. [21] Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka. [22] Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka. [23] Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma. [24] Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. [25] Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye. [26] Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa. [27] Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo. [28] Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa. [29] Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama. [30] Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu. [31] Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru. [32] Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu. [33] Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.
