Miyambo 12:1-28 OCCL
[1] Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa. [2] Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo. [3] Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka. [4] Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake. [5] Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo. [6] Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa. [7] Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe. [8] Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa. [9] Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe. [10] Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza. [11] Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru. [12] Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso. [13] Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto. [14] Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira. [15] Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo. [16] Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa. [17] Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama. [18] Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa. [19] Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa. [20] Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe. [21] Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera. [22] Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona. [23] Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera. [24] Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo. [25] Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa. [26] Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa. [27] Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali. [28] Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
