[1] Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
[2] Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
[3] Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
[4] Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
[5] Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
[6] Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
[7] Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
[8] Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
[9] Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
[10] Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
[11] Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
[12] Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
[13] mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
[14] Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
[15] Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
[16] Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
[17] Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
[18] Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
[19] Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
[20] Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
[21] Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
[22] Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
[23] Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.