Masalimo 94:1-23 OCCL

[1] Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu. [2] Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera. [3] Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe? [4] Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza. [5] Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu. [6] Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye. [7] Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.” [8] Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru? [9] Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona? [10] Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru? [11] Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe. [12] Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu; [13] mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje. [14] Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake. [15] Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata. [16] Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa? [17] Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa. [18] Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza. [19] Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga. [20] Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake? [21] Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe. [22] Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako. [23] Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.