Masalimo 85:1-13 OCCL

[1] Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo. [2] Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. Sela [3] Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa. [4] Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu. [5] Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse? [6] Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu? [7] Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu. [8] Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa. [9] Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu. [10] Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana. [11] Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba. [12] Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake. [13] Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.