Masalimo 80:1-19 OCCL

[1] Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani [2] kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa. [3] Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe. [4] Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu? [5] Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale. [6] Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza. [7] Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe. [8] Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo. [9] Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko. [10] Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake. [11] Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje. [12] Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake? [13] Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya. [14] Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu, [15] muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha. [16] Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka. [17] Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha. [18] Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu. [19] Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.