Masalimo 78:1-72 OCCL

[1] Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga. [2] Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale [3] zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza. [4] Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita. [5] Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo, [6] kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso. [7] Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake. [8] Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye. [9] Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo; [10] iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake. [11] Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa. [12] Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani. [13] Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma. [14] Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse. [15] Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri; [16] Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje. [17] Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu. [18] Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka. [19] Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu? [20] Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?” [21] Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli, [22] pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake. [23] Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba; [24] anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba. [25] Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya. [26] Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake. [27] Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. [28] Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse. [29] Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka. [30] Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe, [31] mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli. [32] Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe. [33] Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso. [34] Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu. [35] Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo. [36] Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo; [37] Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake. [38] Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse. [39] Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso. [40] Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu! [41] Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli. [42] Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza, [43] tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani. [44] Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo. [45] Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza. [46] Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe. [47] Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu. [48] Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani. [49] Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza. [50] Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri. [51] Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu [52] Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu. [53] Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo. [54] Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera. [55] Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo. [56] Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake. [57] Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika. [58] Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo. [59] Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu. [60] Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu. [61] Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani. [62] Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake. [63] Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati; [64] ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira. [65] Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo. [66] Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse. [67] Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu; [68] Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda. [69] Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya. [70] Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa; [71] kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake. [72] Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.