Masalimo 73:1-28 OCCL
[1] Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima. [2] Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa. [3] Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa. [4] Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu. [5] Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse. [6] Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa. [7] Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire. [8] Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.” [9] Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi. [10] Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka. [11] Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?” [12] Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira. [13] Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga. [14] Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse. [15] Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu. [16] Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri [17] kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo. [18] Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke. [19] Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha! [20] Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe. [21] Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga, [22] ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu. [23] Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja. [24] Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero. [25] Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo. [26] Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya. [27] Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu. [28] Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
