Masalimo 70:1-5 OCCL

[1] Fulumirani Mulungu kundipulumutsa; Yehova bwerani msanga kudzandithandiza. [2] Iwo amene akufunafuna moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene akukhumba chiwonongeko changa abwezedwe mopanda ulemu. [3] Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,” abwerere chifukwa cha manyazi awo. [4] Koma onse amene akufunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!” [5] Koma ine ndine wosauka ndi wosowa; bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu. Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga; Inu Yehova musachedwe.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.