Masalimo 63:1-11 OCCL

[1] Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi. [2] Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu. [3] Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani. [4] Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga. [5] Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya. [6] Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku. [7] Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu. [8] Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza. [9] Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi. [10] Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe. [11] Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.