Masalimo 61:1-8 OCCL

[1] Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa. [2] Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo. [3] Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga. [4] Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu. [5] Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu. [6] Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka. [7] Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze. [8] Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.