[1] Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
[2] Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
[3] Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
[4] Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
[5] Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
[6] Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
[7] Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
[8] Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.