Masalimo 49:1-20 OCCL

[1] Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse, [2] anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka: [3] Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru. [4] Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga. [5] Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira. [6] Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo? [7] Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu. [8] Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire, [9] kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda. [10] Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena. [11] Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo. [12] Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama. [13] Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. Sela [14] Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. [15] Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. [16] Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira; [17] Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye. [18] Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino, [19] iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala. [20] Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.