[1] Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
[2] anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
[3] Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
[4] Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
[5] Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
[6] Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
[7] Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
[8] Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
[9] kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
[10] Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
[11] Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
[12] Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
[13] Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. Sela
[14] Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu.
[15] Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini.
[16] Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
[17] Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
[18] Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
[19] iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
[20] Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.