Masalimo 47:1-9 OCCL

[1] Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe. [2] Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi! [3] Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu. [4] Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. Sela [5] Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga. [6] Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando. [7] Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando. [8] Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera. [9] Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.