Masalimo 41:1-13 OCCL

[1] Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka; Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso. [2] Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake; Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake. [3] Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda. [4] Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo; chiritseni pakuti ndakuchimwirani.” [5] Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?” [6] Pamene wina abwera kudzandiona, amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe; kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja. [7] Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane, iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti, [8] “Matenda owopsa amugwira; sadzaukapo pamalo pamene wagona.” [9] Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane. [10] Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere. [11] Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane, pakuti mdani wanga sandigonjetsa. [12] Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya. [13] Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya. Ameni ndi Ameni.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.