[1] Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
[2] Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
[3] Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
[4] Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
[5] tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
[6] Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
[7] Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
[8] Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
[9] Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
[10] Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
[11] Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
[12] Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
[13] Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
[14] Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
[15] Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
[16] Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
[17] Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
[18] Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
[19] Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
[20] Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
[21] Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
[22] Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!